Bungwe la Nudinga Hands Foundation lapeleka thandizo la zovala zakusukulu komaso katundu wina monga shuga, sopo ndi makope kwa ana asukulu omwe ndiosowa m’mapezedwe.
Polankhula ndi Dowa FM Online m’mudzi mwa Kasalika, mfumu yaikulu Mponela m’boma la Dowa m’modzi mwa akuluakulu omwe amayendetsa bungweli a Nefitaly Damalankhunda ati cholinga chachikulu cha bungweli ndi kuonetsa kuti ana akupita kusukulu ndikutiso chiwerengero cha ana omwe akusiila sukulu panjila chachepa m’derali.
Iye anaonjezeraso kuti bungweli lapeleka thandizoli poonanso ndimomwe chiwelengelo cha ana omwe amakhala komaso kusiira sukulu panjila chikukwera kwambili m’derali.
Polankhula pa zokhudza thandizoli a sinyo gulupu Kasalika ati ndiokondwa ndi momwe bungweli laonetsela chidwi chopititsa patsogolo maphunziro potsindika kuti ndi masomphenya awo ndikuona mwana wa derali akupita patali ndi maphunziro ndipo apempha bungweli kuti lisasiyile panjila ntchitoi yomwe ikugwilizana ndi masomphenya a dziko lino achaka cha 2063.
Wolemba Chifuniro Smoke