Phungu wa nyumba ya malamuro wadera lapakati pa boma la Dowa Darlington Harawa wati kukoza misewu ndi gwero lopititsa patsogolo ntchito za chitukuko kudera.
Harawa walankhula izi pa 29 March 2025 pomwe anatenga nawo mbali pa ntchito yokoza misewu yomwe midzi monga Tomasi, Sunduza, Chezini, Chulu 1, Chulu 2 komaso Thendo kwa mfumu yaikulu Mponela m’boma la Dowa.
Iye anatsindika kuti ntchito za malonda zimayenda bwino ngati misewu ili yolongosoka kudera.
Kumbali yake yemwe akudzapikisana nawo pa mpando wa khansala wadelali Kondwani Lisiya wati anachiona chinthu chofunikira kupeleka galimoto yake kuti ithandizile ntchito yotuta mchenga pa ntchitoyi ponena kuti ndi khumbo lake kuona delari likutukuka pa ntchito ya za malonda.
Lisiya wati masomphenya ake otengapo gawo pa ntchito zachitukuko sakuthela pomwepa koma kuonetsetsaso kuti miyoyo ya anthu okhala kumidzi yosiyanasiyana ikutukuka pankhani ya zachuma pomwe wati akangosankhidwa pa udindowu adzaonetsetsa kuti anthu ali ndi mpamba oyambila ma bizinesi awo ndikumakhala odzidalila pa nkhani ya zachuma.
Wolemba Chifuniro Smoke